Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 34:5-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

5. Napsereza mafupa a ansembe pa maguwa a: nsembe ao, nayeretsa Yuda ndi Yerusalemu.

6. Nateronso m'midzi ya Manase, ndi Efraimu, ndi Simeoni, mpaka Nafitali, m'mabwinja mwao mozungulira.

7. Nagumula maguwa a nsembe, naperapera zifanizo ndi mafano osema, nalikha mafano a dzuwa onse m'dziko lonse la Israyeli, nabwerera kumka ku Yerusalemu.

8. Atakhala mfumu tsono zaka khumi mphambu zisanu ndi ziwiri, atayeretsa dziko ndi nyumbayi, anatuma safana mwana wa Azaliya, ndi Maseya kazembe wa mudzi, ndi Yona mwana wa Yoadazi wolemba mbiri, akonze nyumba ya Yehova Mulungu wace.

9. Ndipo anadza kwa Hilikiya wansembe wamkulu, napereka ndarama adabwera nazo ku nyumba ya Mulungu, zimene Alevi osunga pakhomo adasonkhanitsa kuzilandira ku dzanja la Manase ndi Efraimu, ndi kwa otsala onse a Israyeli, ndi kwa Yuda yense, ndi Benjamini, ndi kwa okhala m'Yerusalemu.

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 34