Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 31:6-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Ndi ana a Israyeli ndi Yuda okhala m'midzi ya Yuda, iwonso anabwera nalo limodzi la magawo khumi la ng'ombe, ndi nkhosa, ndi limodzi la magawo khumi la zinthu zopatulika, zopatulikira Yehova Mulungu wao; naziunjika miyuru miyuru,

7. Mwezi wacitatu anayamba kuika miyalo ya miyuruyi, naitsiriza mwezi wacisanu ndi ciwiri.

8. Ndipo pamene Hezekiya ndi akuru ace anadza, naona miyuruyi, analemekeza Yehova, nadalitsa anthu ace Aisrayeli.

9. Pamenepo Hezekiya anafunsana ndi ansembe ndi Alevi za miyuruyi,

10. Ndipo Azariya wansembe wamkuru wa nyumba ya Zadoki anamyankha, nati, Ciyambire anthu anabwera nazo zopereka ku nyumba ya Yehova, tadya, takhuta, ndipo zatitsalira zambiri; pakuti Yehova anadalitsa anthu ace; ndipo suku kucuruka kwa cotsala.

11. Pamenepo Hezekiya anawauza akonze zipinda m'nyumba ya Yehova; nazikonza.

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 31