Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mbiri 29:20-24 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Pamenepo mfumu Hezekiya analawira mamawa, nasonkhanitsa akalonga a m'mudzi, nakwera kumka ku nyumba ya Yehova.

21. Ndipoanabweranazong'ombe zisanundi ziwiri, ndi nkhosa zamphongo zisanu ndi ziwiri ndi ana a nkhosa asanu ndi awiri, ndi atonde asanu ndi awiri, zikhale nsembe yaucimo ya ufumu, ndi ya malo opatulika, ndi ya Yuda. Ndipo anawauza ansembe ana a Aroni azipereke pa guwa la nsembe la Yehova.

22. Momwemo anapha ng'ombezo, ndi ansembe analandira mwazi, nauwaza pa guwa la nsembe, napha nkhosa zamphongozo, nawaza mwazi pa guwa la nsembe; anaphanso ana a nkhosawo, nawaza mwazi pa guwa la nsembe.

23. Pamenepo anayandikiza nao atonde a nsembe yaucimo pamaso pa mfumu ndi msonkhano; ndipo iwo anawasanjika manja ao,

24. ndi ansembewo anawapha, nacita nsembe yaucimo ndi mwazi wao pa guwa la nsembe, kucita cotetezera Aisrayeli onse; pakuti mfumu idauza kuti nsembe yopsereza ndi nsembe yaucimo zikhale za Aisrayeli onse.

Werengani mutu wathunthu 2 Mbiri 29