Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 9:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Elisa mneneriyo anaitana mmodzi wa ana a aneneri, nanena naye, Udzimangire m'cuuno, nutenge nsupa iyi ya mafuta m'dzanja mwako, numuke ku Ramoti Gileadi.

2. Ndipo ukafikako, ukaunguzeko Yehu mwana wa Yehosafati mwana wa Nimsi, nulowe numnyamukitse pakati pa abale ace, nupite naye ku cipinda cam'katimo.

3. Nutenge nsupa ya mafutayo, nuwatsanulire pamutu pace, nunene, Atero Yehova; Ndakudzoza iwe ukhale mfumu pa Israyeli. Utatero, tsegula pakhomo, nuthawe osacedwa,

4. Pamenepo mnyamatayo, ndiye mneneri, anamuka ku Ramoti Gileadi.

5. Nalowa, ndipo taonani, akazembe a khamu alikukhala pansi; nati iye, Ndiri ndi mau kwa inu, kazembe. Nati Yehu, Kwa yani wa ife tonse? Nati iye, Kwa Inu, kazembe.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 9