Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 7:11-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ndipo iye anaitana alonda ena, ndi iwo anafotokozera a m'nyumba ya mfumu.

12. Niuka mfumu usiku, ninena ndi anyamata ace, Ndikufotokozereni m'mene Aaramu aticitira ife. Adziwa kuti tagwidwa ndi njala, laturuka m'misasa, nabisala kuurengo, ndi kuti, Pamene aturuka m'mudzi tidzawagwira ndi moyo ndi kulowa m'mudzimo.

13. Nayankha mmodzi wa anyamata ace, nati, Atenge tsono akavalo otsala asanu, ndiwo otsala m'mudzi; taonani, adzanga unyinji wonse wa Israyeli otsalawo, kapena adzanga unyinji wonse wa Israyeli otsirizika; tiwatumize tione.

14. Motero anatenga magareta awiri ndi akavalo ao; ndipo mfumu inawatumiza alondole khamu la Aaramu, ndi kuti, Mukani mukaone.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 7