Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 6:16-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Nati iye, Usaopa, pakuti okhala pamodzi ndi ife acuruka koposa aja okhala pamodzi ndi iwo.

17. Ndipo Elisa anapemphera, nati, Yehova, mumtsegulire maso ace kuti aone. Pamenepo Yehova anamtsegulira maso mnyamatayo, napenya iye, ndipo taonani, paphiripo panadzala ndi akavalo ndi magareta amoto akumzinga Elisa.

18. Ndipo atatsikira pali iye, Elisa anapemphera kwa Yehova, nati, Mukanthe mtundu uwu ucite khungu. Ndipo iye anawakantha, nawacititsa khungu, monga mwa mau a Elisa.

19. Ndipo Elisa ananena nao, Ngati njira ndi iyi? ngati mudzi ndi uwu? munditsate ine, ndidzakufikitsani kwa munthu mumfunayo; nawatsogolera ku Samariya.

20. Ndipo kunali, pakufika ku Samariya, Elisa anati, Yehova, muwakanganulire awa maso kuti aone. Nawakanganulira Yehova maso ao, naona iwo, ndipo tapenyani, ali pakati pa Samariya.

21. Niti mfumu ya Israyeli kwa Elisa pakuwaona, Atate wanga ndiwakanthe kodi, ndiwakanthe?

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 6