Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 6:12-17 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. Nati mmodzi wa anyamata ace, lai, mbuye wanga mfumu; koma Elisa, mneneriyo ali ku Israyeli, ndiye amafotokozera mfumu ya Israyeli mau muwanena m'kati mwace mwa cipinda canu cogonamo.

13. Nati iye, Kamuoneni komwe ali; ndikatume munthu kumtenga. Ndipo anamuuza kuti, Ali ku Dotana.

14. Pamenepo anatumizako akavalo ndi magareta ndi khamu lalikuru, nafikako usiku, nauzinga mudziwo.

15. Ndipo atalawirira mamawa mnyamata wa munthu wa Mulungu, naturuka, taonani, khamu la nkhondo linazinga mudzi ndi akavalo ndi magareta. Ndi mnyamata wace ananena naye, Kalanga ine, mbuye wanga! ticitenji?

16. Nati iye, Usaopa, pakuti okhala pamodzi ndi ife acuruka koposa aja okhala pamodzi ndi iwo.

17. Ndipo Elisa anapemphera, nati, Yehova, mumtsegulire maso ace kuti aone. Pamenepo Yehova anamtsegulira maso mnyamatayo, napenya iye, ndipo taonani, paphiripo panadzala ndi akavalo ndi magareta amoto akumzinga Elisa.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 6