Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 5:21-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

21. Motero Gehazi anatsata Namani. Ndipo pamene Namani anaona wina alikumthamangira, anatsika pagareta kukomana naye, nati, Nkwabwino kodi?

22. Nati, Kuli bwino. Mbuye wanga wandituma, ndi kuti, Taonani, andifikira tsopano apa anyamata awiri a ana a aneneri, ocokera ku mapiri a Efraimu; muwapatse talente wa siliva, ndi zobvala zosintha ziwiri.

23. Nati Namani, Viole ulandire matalente awiri. Namkangamiza namanga matalente awiri a siliva m'matumba awiri, ndi zobvala zosintha ziwiri, nasenzetsa anyamata ace awiri; iwo anatsogola atazisenza.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 5