Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 4:41-44 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

41. Pamenepo anati, Bwera naoni ufa. Nathira m'nkhalimo; nati, Gawirani anthu kuti adye. Ndipo m'nkhalimo munalibe cowawa.

42. Ndipo anadza munthu kucokera ku Baala Salisa, nabwera nayo mikate ya zipatso zoyamba kwa munthu wa Mulungu, mikate ya barele makumi awiri, ndi ngala zaziwisi za tirigu zosaomba. Ndipo anati, Uwapatse anthu kuti adye.

43. Koma mnyamata wace anati, Ciani? ndigawire amuna zana ici kodi? Koma anati, Uwapatse anthu kuti adye; pakuti atero Yehova, Adzadya nadzasivako.

44. Potero anawagawira, nadya, nasiyapo, monga mwa mau a Yehova.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 4