Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 17:15-31 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

15. Ndipo anakaniza malemba ace, ndi cipangano anacicita ndi makolo ao, ndi mboni zace anawacitira umboni nazo, natsata zopanda pace, nasanduka opanda pace, natsata amitundu owazinga, amene Yehova adawalamulira nao, kuti asacite monga iwowa.

16. Ndipo anasiya malamulo onse a Yehova Mulungu wao, nadzipangira mafano oyenga, ana a ng'ombe awiri, napanga cifanizo, nagwadira khamu lonse la kuthambo, natumikira Baala.

17. Napititsa ana ao amuna ndi akazi kumoto, naombeza ula, nacita zanyanga, nadzigulitsa kucita coipa pamaso pa Yehova, kuutsa mkwiyo wace.

18. Cifukwa cace Yehova anakwiya naye Israyeli kwakukuru, nawacotsa pamaso pace osatsala mmodzi, koma pfuko la Yudalokha.

19. Yudansosanasunga malamulo a Yehova Mulungu wao, koma anayenda m'malemba a Israyeli amene adawaika.

20. Ndipo Yehova anakaniza mbumba yonse ya Israyeli, nawazunza, nawapereka m'dzanja la ofunkha, mpaka anawataya pamaso pace.

21. Pakuti anang'amba Israyeli, kumcotsa ku nyumba ya Davide; ndipo anamlonga mfumu Yerobiamu mwana wa Nebati; Yerobiamu naingitsa Israyeli asatsate Yehova, nawalakwitsa kulakwa kwakukuru.

22. Nayenda ana a Israyeli m'zolakwa zonse za Yerobiamu, zimene anazicita osazileka;

23. mpaka Yehova adacotsa Israyeli pamaso pace, monga adanena mwa dzanja la atumiki ace onse aneneriwo. Momwemo Israyeli anacotsedwa m'dziko lao kumka nao ku Asuri mpaka lero lino.

24. Ndipo mfumu ya Asuri anabwera nao anthu ocokera ku Babulo, ndi ku Kuta, ndi ku Ava, ndi ku Hamati, ndi ku Safaravaimu, nawakhalitsa m'midzi ya Samariya, m'malo mwa ana a Israyeli; nakhala iwo eni ace a Samariya, nakhala m'midzi mwace.

25. Ndipo kunali, poyamba iwo kukhala komweko, sanaopa Yehova; ndipo Yehova anawatumizira mikango, niwapha ena a iwowa.

26. Motero ananena ndi mfumu ya Asuri, kuti, Amitundu aja mudawacotsa kwao, ndi kuwakhalitsa m'midzi ya Samariya, sadziwa makhalidwe a Mulungu wa dzikoli; cifukwa cace anawatumizira mikango pakati pao, ndipo taonani, irikuwapha; popeza sadziwa makhalidwe a Mulungu wa dzikoli.

27. Pamenepo mfumu ya Asuri analamulira, kuti, Mukani naye komweko wina wa ansembe munawacotsako, nakakhale komweko, akawalangize makhalidwe a Mulungu wa dzikoli.

28. Nadza wina wa ansembewo adawacotsa ku Samariya, nakhala ku Beteli, nawalangiza m'mene azimuopera Yehova.

29. Koma a mtundu uli wonse anapanga milungu yao yao, naiika m'nyumba za misanje adazimanga Asamariya, a mtundu uli wonse m'midzi mwao mokhala iwo.

30. Ndipo anthu a Babulo anapanga Sukoti Bemoti, ndi anthu a Kuta anapanga Nerigali, ndi anthu a Hamati anapanga Asima,

31. ndi Aava anapanga Nibazi ndi Tarataka; ndi a Sefaravaimu anawatentha ana ao m'moto kwa Adrameleki, ndi Anameleki, milungu ya Asefaravaimu.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 17