Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

2 Mafumu 10:25-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

25. Ndipo kunali, atatsiriza kupereka nsembe yopsereza, Yehu anati kwa otumikira ndi atsogoleri, Lowani, akantheni; asaturuke ndi mmodzi yense. Nawakantha ndi lupanga lakuthwa; ndi otumikira ndi atsogoleri anawataya kubwalo, namuka ku mudzi wa nyumba ya Baala.

26. Naturutsa zoimiritsa zija zinali m'nyumba ya Baala, nazitentha.

27. Nagamula fane la Baala, nagamula nyumba ya Baala, naiyesa dzala mpaka lero lino.

28. Momwemo Yehu anaononga Baala m'Israyeli.

29. Koma Yehu sanazileka zoipa za Yerobiamu mwana wa Nebati, zimene adacimwitsa nazo Israyeli, ndizo ana a ng'ombe agolidi okhala m'Beteli ndi m'Dani.

Werengani mutu wathunthu 2 Mafumu 10