Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 8:7-11 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

7. Ndipo Yehova ananena ndi Samueli, Umvere mau onse anthuwo alikulankhula nawe; popeza sindiwe anakukana, koma ndine anandikana, kuti ndisakhale mfumu yao.

8. Monga nchito zao zonse anazicita kuyambira tsiku lija ndinawaturutsa ku Aigupto, kufikira lero lino kuti anandisiya Ine, natumikira milungu yina, momwemo alikutero ndi iwenso.

9. Cifukwa cace tsono umvere mau ao koma uwacenjeze kolimba, ndi kuwadziwitsa makhalidwe ace a mfumu imene idzawaweruza.

10. Ndipo Samueli anauza anthu akumpempha iye mfumu mau onse a Yehova,

11. Nati, Awa ndi makhalidwe a mfumu imene idzaweruza inu; idzatenga ana anu amuna, akhale akusunga magareta, ndi akavale ace; ndipo adzathamanga ndi kutsogolera magareta ace;

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 8