Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 8:12-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

12. idzawaika akhale otsogolera cikwi, ndi otsogolera makumi asanu; ndipo idzaika ena kulima minda yace, ndi kutema dzinthu zace, ndi kumpangira zipangizo za nkhondo, ndi zipangizo za magareta.

13. Ndipo idzatenga ana anu akazi apange zonunkhira, naphikire, naumbe mikate.

14. Ndipo idzalanda minda yanu, ndi minda yamphesa yanu, ndi minda yaazitona, inde minda yoposayo, nidzaipatsa anyamata ace.

15. Ndipo idzatenga limodzi la magawo khumi la mbeu zanu, ndi la minda yanu yamphesa, nidzalipatsa akapitao ace, ndi anyamata ace.

16. Ndipo idzatenga akapolo anu, ndi adzakazi anu, ndi anyamata anu okongola koposa, ndi aburu anu, nidzawagwiritsa nchito yace.

17. Idzatenga limodzi la magawo khumi la zoweta zanu; ndipo inu mudzakhala akapoloace.

18. Ndipotsiku lija mudzapfuula cifukwa ca mfumu yanu munadzisankhira nokha; koma Yehova sadzayankha inu tsiku lijalo.

19. Koma anthu anakana kumvera mau a Samueli; nati, Iai, koma tifuna kukhala nayo mfumu yathu;

20. kuti ifenso tikafanane nao anthu a mitundu yonse; kuti mfumu yathuyo ikatiweruzire, ndi kuturuka kutitsogolera, ndi kuponya nafe nkhondo zathu.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 8