Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 8:10-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

10. Ndipo Samueli anauza anthu akumpempha iye mfumu mau onse a Yehova,

11. Nati, Awa ndi makhalidwe a mfumu imene idzaweruza inu; idzatenga ana anu amuna, akhale akusunga magareta, ndi akavale ace; ndipo adzathamanga ndi kutsogolera magareta ace;

12. idzawaika akhale otsogolera cikwi, ndi otsogolera makumi asanu; ndipo idzaika ena kulima minda yace, ndi kutema dzinthu zace, ndi kumpangira zipangizo za nkhondo, ndi zipangizo za magareta.

13. Ndipo idzatenga ana anu akazi apange zonunkhira, naphikire, naumbe mikate.

14. Ndipo idzalanda minda yanu, ndi minda yamphesa yanu, ndi minda yaazitona, inde minda yoposayo, nidzaipatsa anyamata ace.

15. Ndipo idzatenga limodzi la magawo khumi la mbeu zanu, ndi la minda yanu yamphesa, nidzalipatsa akapitao ace, ndi anyamata ace.

16. Ndipo idzatenga akapolo anu, ndi adzakazi anu, ndi anyamata anu okongola koposa, ndi aburu anu, nidzawagwiritsa nchito yace.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 8