Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 7:9-16 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Ndipo Samueli anatenga mwana wa nkhosa woyamwa, nampereka wathunthu kwa Yehova, nsembe yopsereza; ndipo Samueli anapempherera Israyeli kwa Yehova; ndipo Yehova anambvomereza.

10. Ndipo pamene Samueli analikupereka nsembe yopserezayo, Afilisti anayandikira kuti aponyane ndi Aisrayeli; koma tsiku lomwe lija Yehova anagunda ndi kugunda kwakukuru pa Afilistiwo, nawapolonganitsa. Ndipo anakanthidwa pamaso pa Aisrayeli.

11. Ndipo Aisrayeli anaturuka ku Mizipa, nathamangira Afilisti, nawakantha mpaka anafika pansi pa Betikara.

12. Pamenepo Samueli anatenga mwala nauimika pakati pa Mizipa ndi Seni, naucha dzina lace. Ebenezeri, nati, Kufikira pano Yehovaanatithandiza.

13. Comweco anagonjetsa Afilisti, ndino iwo sanatumphanso malire a Israyeli ndipo dzanja la Yehova linasautsa Afilisti masiku onse a Samueli.

14. Ndipo midzi ya Israyeli imene Afilisti adailanda kale inabwezedwa kwa Aisrayeli, kuyambira ku Ekroni kufikira ku Gati; ndi Aisrayeli analanditsa miraga yao m'manja a Afilisti. Ndipo pakati pa Aisrayeli ndi Aamori panali mtendere;

15. ndipo Samueli anaweruza Israyeli masiku onse a moyo wace.

16. Ndipo anayenda cozungulira caka ndi caka ku Beteli, ndi ku Giligala, ndi ku Mizipa; naweruza Israyeli m'malo onse amenewa.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 7