Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 4:3-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Ndipo pamene anthu anafika ku zithandozo, akuru a Israyeli anati, Yehova anatikanthiranji lero pamaso pa Afilisti? Tikadzitengere likasa la cipangano la Yehova ku Silo, kuti likabwera pakati pa ife, lidzatipulumutsa m'dzanja la adani athu.

4. Cifukwa cace anatumiza ku Silo kuti akatenge kumeneko likasalo la cipangano la Yehova wa makamu, wokhala pakati pa akerubi; ndipo ana awiriwo a Eli, Hofeni ndi Pinehasi anali komweko ndi likasa la cipangano la Yehova.

5. Pakufika likasalo la cipangano la Yehova kuzithando, Aisrayeli onse anapfuula ndi mau okweza, kotero kuti dziko linacita cibvomezi.

6. Ndipo Afilistiwo pakumva kubuma pa kupfuula kwao, anati, Phokoso ili la kupfuula kwakukuru ku zithando za Aisrayeli litani? Ndipo anamva kuti likasa la Yehova lidzafika ku zithandozo.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 4