Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 28:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo kunali masiku aja, Afilisti anasonkhanitsa pamodzi makamu ao onse kunkhondo, kuti akaponyane ndi Aisrayeli. Ndipo Akisi ananena ndi Davide, Dziwa kuti zoonadi, udzaturuka nane ndi nkhondo, iwe ndi anthu ako.

2. Ndipo Davide anati kwa Akisi, Potero mudzadziwe cimene mnyamata wanu adzacita. Ndipo Akisi anati kwa Davide, Cifukwa cace ndidzakuika iwe ukhale wondisungira moyo wanga masiku onse.

3. M'menemo Samueli ndipo atafa, ndipo Aisrayeli onse atalira maliro ace, namuika m'Rama, m'mudzi mwao. Ndipo Sauli anacotsa m'dzikomo obwebweta onse, ndi aula onse.

4. Ndipo Afilisti anasonkhana, nadza namanga misasa ku Sunemu; ndipo Sauli anasonkhanitsa Aisrayeli onse, namanga iwo ku Giliboa.

5. Ndipo pamene Sauli anaona khamu la Afilisti, anaopa, ndi mtima wace unanjenjemera kwakukuru.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 28