Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 26:16-19 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Ici unacicita siciri cabwino. Pali Yehova, muyenera kufa inu, cifukwa simunadikira mbuye wanu, wodzozedwa wa Yehova. Ndipo tsono, penyani mkondo wa mfumu ndi cikho ca madzi zinali kumutu kwace ziri kuti?

17. Ndipo Sauli anazindikira mau ace a Davide, nati, Ndi mau ako awa, mwana wanga Davide? Nati Davide, Ndi mau anga mfumu, mbuye wanga.

18. Nati iye, Cifukwa ninji mbuye wanga amalondola mnyamata wace? pakuti ndacitanji? kapena m'dzanja langa muli coipa cotani?

19. Cifukwa cace mbuye wanga mfumu amvere mau a kapolo wace. Ngati ndi Yehova anakuutsirani inu kutsutsana ndi ine, alandire copereka; koma ngati ndi ana a anthu, atembereredwe pamaso pa Yehova, pakuti anandipitikitsa lero kuti ndisalandireko colowa ca Yehova, ndi kuti, Muka, utumikire milungu yina.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 26