Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 23:9-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

9. Ndipo Davide anadziwa kuti Sauli analikulingalira zomcitira zoipa; nati kwa Abyatara wansembe, Bwera kuno ndi efodi.

10. Nati Davide, Yehova, Mulungu wa Israyeli, mnyamata wanu wamva zoona kuti Sauli afuna kudza ku Keila, kuononga mudziwo cifukwa ca ine.

11. Kodi amuna a ku Keila adzandipereka m'dzanja lace? Kodi Sauli adzatsikira ndithu, monga mnyamata wanu wamva? Yehova Mulungu wa Israyeli, ndikupemphani, muuze mnyamata wanu. Ndipo Yehova anati, Adzatsika.

12. Tsono Davide anati, Kodi amuna a ku Keila adzandipereka ine ndi anyamata anga m'dzanja la Sauli? Ndipo Yehova anati, Adzakupereka.

13. Potero Davide ndi anyamata ace, ndiwo monga ngati mazana asanu ndi limodzi, ananyamuka, naturuka ku Keila, nayendayenda kuli konse adakhoza kuyendako. Ndipo anauza Sauli kuti Davide wapulumuka ku Keila; iye naleka kumtsata.

14. Ndipo Davide anakhala m'cipululu m'ngaka, nakhala m'dziko la mapiri m'cipululu ca Zifi. Ndipo Sauli anamfunafuna masiku onse, koma Mulungu sadampereka m'dzanja lace.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 23