Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 22:3-9 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Ndipo Davide anacoka kumeneko kunka ku Mizipa wa ku Moabu; nati kwa mfumu ya Moabu, Mulole atate wanga ndi mai wanga aturuke nakhale nanu, kufikira ndidziwa cimene Mulungu adzandidtira.

4. Ndipo anawatenga kumka nao pamaso pa mfumu ya Moabu; ndipo iwo anakhala naye nthawi yonse Davide anali ku lingalo.

5. Ndipo mneneri Gadi anati kwa Davide, Musamakhala m'lingamo; cokani, mulowe m'dziko la Yuda. Potero Davide anacokako, nafika ku nkhalango ya Hereti.

6. Pakumva Sauli kuti anadziwika Davide, ndi anthu ace akukhala naye, Sauti analikukhala m'Gibeya, patsinde pa mtengo wa kumsanje, m'dzanja lace munali mkondo wace, ndi anyamata ace onse anaimirira pali iye.

7. Ndipo Sauli anati kwa anyamata ace akuima comzinga, Imvani tsopano, inu a Benjamini; kodi mwana wa Jese adzakupatsani inu nonse minda, ndi minda yamphesa, kodi adzakuikani mukhale atsogoleri a zikwi ndi a mazana;

8. kuti inu nonse munapangana dwembu pa ine, ndipo palibe wina wakundiululira kuti mwana wanga anapangana pangano ndi mwana wa Jese, ndipo palibe wilia wa inu wakundidtira cifundo kapena kundidziwitsa kuti mwana wanga anafulumiza mnyamata wanga kundilalira monga lero lomwe?

9. Pamenepo Doegi wa ku Edomu, anaimirira ndi anyamata a Sauli, nayankha, nati, Ine ndinamuona mwana wa Jeseyo alikufika ku Nobi, kwa Ahimeleki mwana wa Ahitubu.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 22