Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 20:8-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. Cifukwa cace ucitire kapolo wako zokoma mtima; popeza wamcititsa kapolo wako kupangana nawe pangano la kwa Yehova; koma ngati mwa ine muli coipa ciri conse, undiphe wekha; udzapita nane bwanji kwa atate wako?

9. Ndipo Jonatani anati, lai ndi pang'ono ponse; ine ndikadziwa konse kuti atate wanga anatsimikiza mtima kukucitira coipa, sindidzadziwitsa iwe kodi?

10. Tsono Davide anati kwa Jonatani, Adzandiuza ndani ngati atate wako alankhulira iwe mokalipa?

11. Nati Jonatani kwa Davide, Tiyeni timuke kuthengo. Namuka onse awiri kuthengoko.

12. Ndipo Jonatani anati kwa Davide, Yehova, Mulungu wa Israyeli, akhale mboni; nditaphera mwambi atate wanga mawa dzuwa lino, kapena mkuca, onani, pakakhala kanthu kabwino kakucitira Davide, sindidzakutumira mthenga ndi kukuululira kodi?

13. Mulungu alange Jonatani, ndi kuonjezapo, ngati atate wanga akondwera kukucitira coipa, ine osakuululira, ndi kukucotsa kuti upite mumtendere; ndipo Yehova akhale nawe, monga anakhala naye atate wanga.

14. Ndipo undionetsere cifundo ca Yehova, si pokhala ine ndi moyo pokha, kuti ndingafe;

15. komanso usaleke kucitira cifundo a m'nyumba yanga nthawi zonse; mungakhale m'tsogolomo Yehova atathera adani onse a Da vide pa dziko lapansi.

16. Comweco Jonatani anapangana pangano ndi nyumba ya Davide, ndipo Yehova anakwaniritsa izi polanga adani a Davide.

17. Ndipo Jonatani anamlumbiritsa Davide kaciwiri, cifukwa anamkonda; popeza anamkonda monga anakonda moyo wa iye yekha.

18. Tsono Jonatani ananena kwa Davide, Mawa mwezi ukhala; ndipo adzakufuna, popeza udzasoweka pamalo pako.

19. Ndipo atapita masiku atatu, utsike msanga, nufike kumene unabisala tsiku la mrandu uja, nukhale pa mwala wa Ezeri.

20. Ndipo ine ndidzaponya mibvi itatu pambali pace, monga ngati ndirikuponya pacandamali.

21. Ndipo taona, ndidzatumiza mnyamatayo, ndi kuti, Kafune mibviyo, Ndikamuuza mwanayo, kuti, Taona mibvi iri cakuno; uitole nubwere, popeza pali mtendere kwa iwe, palibe kanthu, pali Yehova.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 20