Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 2:35-36 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

35. Ndipo ndidzadziukitsira wansembe wokhulupirika, amene adzacita monga cimene ciri mumtima mwanga ndi m'cifuniro canga; ndipo ndidzammangira nyumba yokhazikika, ndipo iyeyu adzayenda pamaso pa wodzozedwa wanga masiku onse.

36. Ndipo kudzali kuti yense wakusiyidwa wa m'banja lako adzabwera kwa iye nadzawerama ndi kupempha ndalama ndi cakudya, nadzati, Mundipatsetu nchito yina ya wansembe, kuti ndikaona kakudya.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 2