Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 18:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo kunali, pakutsiriza iye kulankhula ndi Sauli, mtima wa Jonatani unalumikizika ndi mtima wa Davide, ndipo Jonatani anamkonda iye monga moyo wa iye yekha.

2. Ndipo Sauli anamtenga tsiku lomwelo, osamlolanso apite kwao kwa atate wace.

3. Pamenepo Jonatani ndi Davide anapangana pangano, pakuti adamkonda iye ngati moyo wa iye yekha.

4. Ndipo Jonatani anabvula maraya ace anali nao, napatsa Davide, ndi zobvala zace, ngakhale lupanga lace, ndi uta wace, ndi lamba lace.

5. Ndipo Davide anaturuka kunka kuli konse Sauli anamtumako, nakhala wocenjera; ndipo Sauli anamuika akhale woyang'anira anthu a nkhondo; ndipo ici cinakomera anthu onse, ndi anyamata a Sauli omwe.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 18