Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 15:20-35 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

20. Ndipo Sauli ananena ndi Samueli, Koma ndinamvera mau a Yehova, ndipo ndinayenda njira Yehova anandituma ine, ndipo ndinabwera naye Agagi mfumu ya Amaleki, ndi Aamaleki ndinawaononga konse konse.

21. Koma anthuwo anatengako zowawanya, nkhosa ndi ng'ombe, zoposa za zija tidayenera kuziononga, kuziphera nsembe kwa Yehova Mulungu wanu ku Giligala.

22. Ndipo Samueli anati, Kodi Yehova akondwera ndi nsembe zopsereza ndi nsembe zophera, monga ndi kumvera mau a Yehova? Taonani, kumvera ndiko kokoma koposa nsembe, kuchera khutu koposa mafuta a nkhosa zamphongo,

23. Pakuti kupanduka kuli ngati coipa ca kucita nyanga, ndi mtima waliuma uli ngati kupembedza milungu yacabe ndi maula. Popeza inu munakaniza mau a Yehova, Iyenso anakaniza inu, kuti simudzakhalanso mfumu.

24. Ndipo Sauli anati kwa Samueli, Ndinacimwa; pakuti ndinalumpha lamulo la Yehova, ndi mau anu omwe; cifukwa ndinaopa anthuwo, ndi kumvera mau ao.

25. Cifukwa cace tsono, mukhululukire cimo langa, nimubwerere pamodzi ndi ine, kuti ndikalambire Yehova.

26. Ndipo Samueli ananena ndi Sauli, Ine sindibwerera nanu; pakuti munakaniza mau a Yehova, ndipo Yehova anakaniza inu, kuti simudzakhalanso mfumu ya Israyeli.

27. Ndipo pakupotoloka Samueli kuti acoke, iye anagwira cilezi ca mwinjiro wace, ndipo cinang'ambika.

28. Ndipo Samueli ananena naye, Yehova anang'amba ufumu wa Israyeli lero kuucotsa kwa inu, naupatsa kwa mnansi wanu wina wabwino woposa inu.

29. Ndiponso Wamphamvu wa Israyeli sanama kapena kulapa; popeza iye sali munthu kuti akalapa.

30. Pomwepo iye anati, Ndinacimwa, koma mundicitire ulemu tsopano pamaso pa akuru a anthu anga, ndi pamaso pa Israyeli, nimubwerere pamodzi ndi ine, kuti ndikalambire Yehova Mulungu wanu.

31. Comweco Samueli anabwerera natsata Sauli; ndi Sauli analambira Yehova.

32. Ndipo Samueli anati, Bwerani naye kwa ine kuno Agagi mfumu ya Aamaleki. Ndipo Agagi anabwera kwa iye mokondwera. Nati Agagi, Zoonadi kuwawa kwa imfa kunapitirira.

33. Ndipo Samueli anati, Monga lupanga lako linacititsa akazi ufedwa, momwemo mai wako adzakhala mfedwa mwa akazi. Ndipo Samueli anamdula Agagi nthuli nthuli pamaso pa Yehova ku Giligala.

34. Pamenepo Samueli ananka ku Rama; ndi Sauli anakwera kunka ku nyumba yace ku Gibeya wa Sauli.

35. Ndipo Samueli sanadzanso kudzaona Sauli kufikira tsiku la imfa yace; koma Samueli analira cifukwa ca Sauli; ndipo Yehova anali ndi cisoni kuti anamlonga Sauli mfumu ya Israyeli.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 15