Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 14:41-46 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

41. Cifukwa cace Sauli ananena ndi Yehova, Mulungu wa Israyeli, muonetse coonadi. Ndipo maere anagwera Sauli ndi Jonatani; koma anthuwo anapulumuka.

42. Ndipo Sauli anati, Mucite maere pakati pa ine ndi Jonatani mwana wanga. Ndipo anagwera Jonatani.

43. Pamenepo Sauli ananena ndi Jonatani, Undiuze cimene unacita. Ndipo Jonatani anamuuza, nati, Zoonadi ndinangolawako uci pang'ono ndi nsonga ya ndodo inali m'dzanja langa: ndipo onani ndiyenera kufa.

44. Pamenepo Sauli anati, Mulungu andilange, naoniezereko, pakuti udzafa ndithu, Jonatani.

45. Ndipo anthuwo ananena ndi Sauli, Kodi Jonatani adzafa, amene anacititsa cipulumutso cacikuru ici m'Israyeli? Musatero. Pali Yehova, palibe tsitsi limodzi la pa mutu wace lidzagwa pansi, pakuti iye anagwirizana ndi Mulungu lero. Comweco anthuwo anapulumutsa Jonatani kuti angafe. Ndipo Sauli analeka kuwapitikitsa Afilistiwo;

46. ndi Afilistiwo anamuka ku malo a iwo okha.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 14