Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Samueli 10:3-7 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

3. Mukapitirira pamenepo tsono ndi kufika ku mtengo wathundu wa ku Tabori, kumeneko adzakomana nanu anthu atatu akukwera kwa Mulungu ku Beteli, wina wonyamula ana a mbuzi atatu, wina mikate itatu, wina thumba la vinyo.

4. Iwowa adzakulankhulani, ndi kukupatsani mikate iwiri; imeneyi mudzailandira m'manja mwao.

5. Ndipo m'tsogolo mwace mudzafika ku phiri la Mulungu, kumene kuli kaboma ka Afilisti; ndipo kudzali kuti pakufika inu kumudziko mudzakomana ndi gulu la aneneri, alikutsika kumsanje ndi cisakasa, ndi lingaka, ndi toliro, ndi zeze, pamaso pao; iwo adzanenera;

6. ndipo Mzimu wa Yehova udzagwera inu kolimba, nanunso mudzanenera pamodzi nao, nimudzasandulika munthu wina.

7. Ndipo zitakufikirani zizindikilo izi mudzacita monga mudzaona pocita, pakuti Mulungu ali nanu.

Werengani mutu wathunthu 1 Samueli 10