Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 8:23-28 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Yehova Mulungu wa Israyeli, palibe Mulungu wolingana ndi inu m'thambo la kumwamba, kapena pa dziko lapansi, wakusungira cipangano ndi cifundo akapolo anu akuyenda ndi mtima wonse pamaso panu,

24. wakusungira mtumild wanu Davide atate wanga cimene mudamlonjezaco; munalankhulanso m'kamwa mwanu ndi kukwaniritsa ndi dzanja lanu monga lero lino.

25. Ndipo tsopano, Yehova Mulungu wa Israyeli, msungireni mtumiki wanu Davide atate wanga cimene cija mudamlonjezaco, ndi kuti, Sadzakusowa munthu pamaso panga wokhala pa mpando wacifumu wa Israyeli; komatu ana ako acenjere njira yao, kuti akayende pamaso panga monga umo unayendera iwe pamaso panga.

26. Ndipo tsopano, Mulungu wa Israyeli, atsimikizike mau anu amene munalankhula ndi mtumiki wanu Davide atate wanga.

27. Kodi Mulungu adzakhala ndithu pa dziko lapansi? Taonani, thambo ndi m'Mwambamwamba zicepa kukulandirani, koposa kotani nanga nyumba iyi ndaimangayi.

28. Koma muceukire pemphero la kapolo wanu, ndi pembedzero lace, Yehova Mulungu wanga, kumvera kulira ndi kupempha kwace kumene kapolo wanu apempha pamaso panu lero;

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 8