Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 8:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Pamenepo Solomo anasonkhanitsa akulu a Israyeli, ndi akulu onse a mafuko, akalonga a nyumba za atate a ana a Israyeli, kwa mfumu Solomo m'Yerusalemu, kukatenga likasa la cipangano ca Yehova m'mudzi wa Davide, ndiwo Ziyoni.

2. Ndipo anthu onse a Israyeli anasonkhana kwa mfumu Solomo kukadyereram'mwezi wa Etanimu, ndiwo mwezi wacisanu ndi ciwiri.

3. Ndipo akulu onse a Israyeli anadza, ansembe nanyamula likasa.

4. Ndipo anatenga likasa la Yehova, ndi cihema cokomanako, ndi zipangizo zonse zopatulika, zinali m'cihemamo, inde zimenezi anazitenga ansembe ndi Alevi.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 8