Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 4:25-30 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

25. Ndipo Ayuda ndi Aisrayeli anakhala mosatekeseka, munthu yense patsinde pa mpesa wace ndi mkuyu wace, kuyambira ku Dani mpaka ku Beeriseba, masiku onse a Solomo.

26. Ndipo Solomo anali nazo zipinda za akavalo a magareta ace zikwi makumi anai, ndi apakavalo zikwi khumi mphambu ziwiri.

27. Ndipo akapitao aja anatengetsera cakudya Solomo ndi anthu onse akudya ku gome la mfumu Solomo, munthu yense m'mwezi mwace, sanalola kanthu kasoweke.

28. Barelenso ndi udzu wa akavalo ndi ngamila anabwera nazo kumalo kwao, munthu yense monga momwe anamuuzira.

29. Ndipo Mulungu anampatsa Solomo nzeru ndi luntha lambiri, ndi mtima wodziwa za mitundu mitundu, zonga mcenga uli m'mbali mwa nyanja.

30. Ndipo nzeru ya Solomo inaposa nzeru za anthu onse a kum'mawa, ndi nzeru zonse za ku Aigupto.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 4