Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 3:16-23 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Pamenepo analowa kwa mfumu akazi awiri, ndiwo adama, naima pamaso pace.

17. Ndipo mkazi mmodzi anati, Mbuye wanga, ine ndi mkazi uyu tikhala awiri m'nyumba imodzi; ndipo ine ndinaona mwana, iye ali m'nyumbamo.

18. Ndipo kunacitika kuti tsiku lacitatu nditaona ine mwana, mnzangayu anaonanso mwana; ndipo ife tinali pamodzi, munalibe mlendo ndi ife m'nyumbamo, koma ife awiri m'nyumbamo.

19. Ndipo mwana wa mnzangayu anamwalira usiku, pokhala iyeyu anamgonera.

20. Ndipo iye anauka pakati pa usiku, natenga mwana wanga kumimba kwanga, mdzakazi wanu ndiri m'tulo, namuika m'mfukato mwace, naika mwana wace wakufa m'mfukato mwanga.

21. Ndipo pouka ine m'mawa kuyamwitsa mwana wanga ndaona ngwakufa, koma nditamzindikira m'mawa ndaona si mwana wanga wobala ine ai.

22. Ndipo mkazi winayo anati, lai, koma wamoyoyu ndi mwana wanga, ndi wakufayu ndi mwana wako. Ndipo uja anati, lai, koma wakufayu ndi mwana wako, ndi wamoyoyu ndi mwana wanga. Motero iwo analankhula pamaso pa mfumu.

23. Tsono mfumu inati, Uyu akuti, Wamoyoyu ndiye mwana wanga ndi wakufayu ndiye mwana wako; ndipo winayo akuti, lai, koma mwana wako ndiye wakufayu, ndi mwana wanga ndiye wamoyoyu.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 3