Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 3:14-21 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

14. Ndipo ukadzayenda m'njira zanga kusunga malemba anga ndi malamulo anga, monga atate wako Davide anayendamo, Ine ndidzacurukitsa masiku ako.

15. Ndipo Solomo anauka, ndipo taona, ndilo loto; nabwera ku Yerusalemu, naima ku likasa la cipangano ca Yehova, napereka nsembe zopsereza ndi nsembe zamtendere, nakonzera anyamata ace onse madyerero.

16. Pamenepo analowa kwa mfumu akazi awiri, ndiwo adama, naima pamaso pace.

17. Ndipo mkazi mmodzi anati, Mbuye wanga, ine ndi mkazi uyu tikhala awiri m'nyumba imodzi; ndipo ine ndinaona mwana, iye ali m'nyumbamo.

18. Ndipo kunacitika kuti tsiku lacitatu nditaona ine mwana, mnzangayu anaonanso mwana; ndipo ife tinali pamodzi, munalibe mlendo ndi ife m'nyumbamo, koma ife awiri m'nyumbamo.

19. Ndipo mwana wa mnzangayu anamwalira usiku, pokhala iyeyu anamgonera.

20. Ndipo iye anauka pakati pa usiku, natenga mwana wanga kumimba kwanga, mdzakazi wanu ndiri m'tulo, namuika m'mfukato mwace, naika mwana wace wakufa m'mfukato mwanga.

21. Ndipo pouka ine m'mawa kuyamwitsa mwana wanga ndaona ngwakufa, koma nditamzindikira m'mawa ndaona si mwana wanga wobala ine ai.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 3