Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 21:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo zitatha izi, kunaoneka zotere: Naboti wa ku Yezreeli anali ndi munda wamphesa, unali m'Yezreelimo, m'mbali mwa nyumba ya Ahabu mfumu ya ku Samaria.

2. Ndipo Ahabu analankhula ndi Naboti, nati, diloleni Ndipatse munda wako wamphesa ukhale munda wanga wa ndiwo, popeza uli pafupi ndi nyumba yanga; ndipo m'malo mwace ndidzakupatsa munda wamphesa wokoma woposa uwu; kapena kukakukomera ndidzakupatsa ndalama za pa mtengo wace,

3. Ndipo Naboti anati kwa Ahabu, Pali Yehova, ndi pang'ono ponse ai, kuti ndikupatseni colowa ca makolo anga,

4. Ndipo Ahabu analowa m'nyumba mwace wamsunamo ndi wokwiya, cifukwa ca mau amene Naboti wa ku Yezreeli adalankhula naye; popeza adati, Sindikupatsani colowa ca makolo anga. M'mwemo anagona pa kama wace, nayang'ana kumbali, nakana kudya mkate.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 21