Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 2:39-46 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

39. Ndipo kunacitika, zitapita zaka zitatu, kuti akapolo awiri a Simeyi anathawira kwa Akisi mwana wa Maaka mfumu ya Gati. Ndipo anamuuza Simeyi, nati, Taonani, akapolo anu akhala ku Gati.

40. Ndipo Simeyi ananyamuka, namangirira mbereko pa buru wace, namka ku Gati kwa Akisi kukafuna aka polo ace; namuka Simeyi, nabwera nao akapolo ace kucokera ku Gati.

41. Ndipo anamuuza Solomo, kuti, Simeyi wacoka ku Yerusalemu kumka ku Gati, nabweranso.

42. Ndipo mfumu inatuma munthu kukaitana Simeyi, niti kwa iye, Kodi sindinakulumbiritsa pa Yehova ndi kukucenjeza, kuti, Tadziwa ndithu, kuti tsiku lakuturuka iwe ndi kukayenda kwina konse udzafa ndithu? Ndipo iwe unati kwa ine, Mau amene ndawamva ndi abwino.

43. Sunasunga cifukwa ninji lumbiro la pa Yehova, ndi lamulo lija ndinakulamulira iwe?

44. Tsono mfumu inanenanso ndi Simeyi, Udziwa iwe coipa conse mtima wako umadziwaco, cimene udacitira Davide atate wanga; cifukwa cace Yehova adzakubwezera coipa cako pamutu pako mwini.

45. Koma mfumu Solomo adzadalitsika, ndi mpando wacifumu wa Davide udzakhazikika pamaso pa Yehova ku nthawi yamuyaya.

46. Pamenepo mfumu inalamulira Benaya mwana wa Yehoyada, ndipo iye anaturuka namkwera, namwalira iye. Ndipo ufumu unakhazikika m'dzanja la Solomo.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 2