Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 2:11-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

11. Ndipo masiku ace akukhala Davide mfumu ya Israyeli anali zaka makumi anai; zaka zisanu ndi ziwiri anakhala mfumu ku Hebroni, ndi zaka makumi atatu mphambu citatu anakhala mfumu ku Yerusalemu.

12. Tsono Solomo anakhala pa mpando wacifumu wa Davide atate wace, ndipo ufumu wace unakhazikika kwakukuru.

13. Pomwepo Adoniya mwana wa Hagati anadza kwa Batiseba amai wace wa Solomo, ndipo mkaziyo anati, Kodi wadza ndi mtendere? Nati, Ndi mtendere umene.

14. Anatinso, Ndiri nanu mau, Nati iye, Tanena.

15. Nati iye, Mudziwa kuti ufumu unali wanga, ndi kuti Aisrayeli onse anaika maso ao pa ine, kuti ndikhale mfumu ndine; koma ufumu watembenuka nukhala wa mbale wanga, popeza iye anaulandira kwa Mulungu.

16. Ndipo tsopano, ndikupemphani pempho limodzi, musandikaniza. Ndipo mkaziyo anati kwa iye, Tanena.

17. Nati iye, Mundinenere kwa mfumu Solomo, popeza sakukanizani, kuti andipatse Abisagi wa ku Sunamu akhale mkazi wanga.

18. Ndipo Batiseba anati, Cabwino, ndidzakunenera kwa mfumu.

19. Tsono Batiseba ananka kwa mfumu Solomo kukanenera Adoniya kwa iye. Ndipo mfumu inanyamuka kukomana naye, namuweramira nakhalanso pa mpando wace wacifumu, naikitsa mpando wina wa amace wa mfumu, nakhala iye ku dzanja lace lamanja.

20. Pamenepo mkaziyo anati, Ndikupemphani kapempho kamodzi, musandikaniza. Ndipo mfumu inati kwa iye, Tapemphani amai wanga, popeza sindikukanizani.

21. Ndipo iye anati, Abisagi wa ku Sunamu apatsidwe kwa Adoniya mbale wanu akhale mkazi wace.

22. Ndipo mfumu Solomo anayankha, nati kwa amai wace, Mupempheranji Abisagi wa ku Sunamu akhale wace wa Adoniya? Mumpempherenso ufumu, popeza ndiye mkuru wanga; inde ukhale wace, ndi wa Abyatara wansembeyo, ndi wa Yoabu mwana wa Zeruya.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 2