Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 16:32-34 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

32. Nammangira Baala guwa la nsembe m'nyumba ya Baala anaimanga m'Samaria.

33. Ahabu anapanganso cifanizo; ndipo Ahabu amene anapambana mafumu onse a Israyeli adamtsogolerawo, kuputa mkwiyo wa Yehova Mulungu wa Israyeli,

34. M'masiku ace Hiyeli wa ku Beteli anamanga Yeriko; pokhazika maziko ace anadzifetsera Abiramu mwana wace woyamba, poimika zitseko zace anadzifetsera Zegubi mwana wace wotsiriza; monga mwa mau a Yehova amene ananenetsa Yoswa mwana wa Nuni.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 16