Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 16:30-34 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

30. Ndipo Ahabu mwana wa Omri anacimwa pamaso pa Yehova koposa onse adamtsogolerawo.

31. Ndipo kunali monga ngati kunamcepera kuyenda m'macimo a Yerobiamu mwana wa Nebati, iye anakwatira Yezebeli mwana wamkazi wa Etibaala mfumu ya Azidoni, natumikira Baala, namgwadira,

32. Nammangira Baala guwa la nsembe m'nyumba ya Baala anaimanga m'Samaria.

33. Ahabu anapanganso cifanizo; ndipo Ahabu amene anapambana mafumu onse a Israyeli adamtsogolerawo, kuputa mkwiyo wa Yehova Mulungu wa Israyeli,

34. M'masiku ace Hiyeli wa ku Beteli anamanga Yeriko; pokhazika maziko ace anadzifetsera Abiramu mwana wace woyamba, poimika zitseko zace anadzifetsera Zegubi mwana wace wotsiriza; monga mwa mau a Yehova amene ananenetsa Yoswa mwana wa Nuni.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 16