Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 16:16-22 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

16. Koma anthu aja omangira misasa anamva kuti Zimri wacita ciwembu, nakanthanso mfumu; cifukwa cace tsiku lomwelo Aisrayeli onse a kumisasa anamlonga Omri kazembe wa nkhondo akhale mfumu ya Israyeli.

17. Ndipo Omri anacoka ku Gibetoni, ndi Aisrayeli onse naye, nakamangira misasa Tiriza.

18. Kunali tsono, pakuona Zimri kuti nkhondo yalowa m'mudzi, anakwera pa nsanja ya nyumba ya mfumu, nadzitenthera ndi mota nyumba ya mfumu, nafa;

19. cifukwa ca macimo ace anacimwawo, pakucita coipa pamaso pa Yehova; popeza anayenda m'njira ya Yerobiamu, ndi m'chimo lace anacimwa nalolo, nacimwitsa nalo Aisrayeli.

20. Macitidwe ena tsono a Zimri, ndi ciwembu anacicitaco, kodi sizilembedwa m'buku la macitidwe a mafumu a Israyeli?

21. Pamenepo anthu a Israyeli anagawika pakati, anthu ena anatsata Tibini mwana wa Ginati kumlonga ufumu, ena natsata Omri.

22. Koma anthu akutsata Omri anapambana iwo akutsata Tibini mwana wa Ginati; nafa Tibini, Omri nakhala mfumu.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 16