Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

1 Mafumu 10:23-29 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Ndipo mfumu Solomo anawaposa mafumu onse a dziko lapansi pa cuma ndi nzeru.

24. Ndipo anthu onse a pa dziko anafuna nkhope ya Solomo, kudzamva nzeru zace zimene Mulungu analonga m'mtima mwace.

25. Ndipo akafika munthu yense ndi mtulo wace, zotengera zasiliva, ndi zotengera zagolidi, ndi zobvala, ndi zida, ndi zonunkhira, ndi akavalo, ndi nyuru; momwemo caka ndi caka.

26. Ndipo Solomo anasonkhanitsa, magareta ndi apakavalo; anali nao magareta cikwi cimodzi mphambu, mazana anai, ndi apakavalo zikwi khumi mphambu ziwiri, nawasungira m'midzi yosungamo magareta, ndi kwamfumu m'Yerusalemu.

27. Ndipo mfumu inacurukitsa siliva ngati miyala m'Yerusalemu, ndi mitengo yamikungudza anailinganiza ndi mikuyu ya m'madambo.

28. Ndipo akavalo a Solomo anacokera ku Aigupto; anthu a malonda a mfumu anawagula magulu magulu, gulu liri lonse mtengo wace.

29. Ndipo gareta limodzi linacokera kuturuka m'Aigupto mtengo wace masekeli a siliva mazana asanu ndi limodzi, ndi kavalo mtengo wace masekeli zana limodzi mphambu makumi asanu; momwemonso iwo anawagulira mafumu onse a Ahiti ndi mafumu a Aramu.

Werengani mutu wathunthu 1 Mafumu 10