3. ndipo popeza anali wa nchito imodzimodzi, anakhala nao, ndipo iwowa anagwira nchito; pakuti nchito yao inali yakusoka mahema.
4. Ndipo anafotokozera m'sunagogemasabata onse, nakopa Ayuda ndi Ahelene.
5. Koma pamene Sila ndi Timoteo anadza potsika ku Makedoniya, Paulo anapsinjidwa ndi mau, nacitira umboni kwa Ayuda kuti Yesu ndiye Kristu.
6. Koma pamene iwo anamkana, nacita mwano, anakutumula maraya ace, nati kwa iwo, Mwazi wanu ukhale pa mitu yanu; ine ndiribe kanthu; kuyambira tsopano ndinka kwa amitundu.