10. Ndipo anthuwo anatero; natenga ng'ombe ziwiri zamkaka, nazimanga pagareta, natsekera anao kwao;
11. naika likasa la Yehova pagaretapo, ndi bokosi m'mene munali mbewa zagolidi ndi zifanizo za mafundo ao.
12. Ndipo ng'ombezo zinatsata njira yolunjika ku Betisemesi, niziyenda mumseu, zirikulira poyenda; sizinapambukira ku dzanja lamanja, kapena kulamanzere; ndipo mafumu a Afilisti anazitsatira kufikira ku malire a Betisemesi.
13. Ndipo a ku Betisemesi analikumweta tirigu wao m'cigwamo; natukula maso ao, naona likasalo, nakondwerapakuliona.