Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yuda 1:4-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

4. Pakuti pali anthu ena anakwawira m'tseri, ndiwo amene aja adalembedwa maina ao kale, kukalandira citsutso ici, anthu osapembedza, akusandutsa cisomo ca Mulungu wathu cikhale cilak olako conyansa, nakaniza Mfumu wayekha, ndi Ambuye wathu, Yesu Kristu.

5. Koma ndifuna kukukumbutsani mungakhale munadziwa zonse kale kuti Ambuye, atapulumutsa mtundu wa anthu ndi kuwaturutsa m'dziko La Aigupto, anaononganso iwo osakhulunirira.

6. Angelonso amene sanasunga cikhalidwe cao coyamba, komatu anasiya pokhala pao pao, adawasunga m'ndende zosatha pansi pa mdima, kufikira ciweruziro ca tsiku lalikuru.

Werengani mutu wathunthu Yuda 1