Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yuda 1:1-4 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. YUDA, kapolo wa Yesu Kristu, ndi mbale wa Yakobo, kwa iwo oitanidwa, okondedwa mwa Mulungu Atate, ndi osungidwa ndi Yesu Kristu:

2. Cifundo ndi mtendere ndi cikondi zikucurukireni.

3. Okondedwa, pakucira cangu conse cakukulemberani za cipulumutso ca ife tonse, ndafulumidwa mtima ine kukulemberani ndi kudandaulira kuti mulimbanetu cifukwa ca cikhulupiriro capatsidwa kamodzi kwa oyera mtima.

4. Pakuti pali anthu ena anakwawira m'tseri, ndiwo amene aja adalembedwa maina ao kale, kukalandira citsutso ici, anthu osapembedza, akusandutsa cisomo ca Mulungu wathu cikhale cilak olako conyansa, nakaniza Mfumu wayekha, ndi Ambuye wathu, Yesu Kristu.

Werengani mutu wathunthu Yuda 1