Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Yohane 18:23-39 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

23. Yesu anayankha iye, Ngati ndalankhula coipa, cita umboni wa coipaco, koma ngati bwino, undipandiranji?

24. Koma Anasi adamtumiza iye womangidwa kwa Kayafa mkulu wa ansembe.

25. Koma Simoni Petro analikuimirira ndi kuotha moto. Pomwepo anati kwa iye, Suli iwenso wa akuphunzira ace kodi? Iyeyu anakana, nati, Sindine.

26. Mmodzi wa akapolo a mkulu wa ansembe ndiye mbale wace wa uja amene Petro anamdula khutu, ananena, Ine sindinakuona iwe kodi m'munda pamodzi ndi iye?

27. Pamenepo Petro anakananso; ndipo pomwepo analira tambala.

28. Pamenepo anamtenga Yesu kucokera kwa Kayafa kupita ku Pretorio; koma munali mamawa; ndipo iwo sanalowa ku Pretorio, kuti angadetsedwe, koma kuti akadye Paskha.

29. Cifukwa cace Pilato anaturukira kunja kwa iwo, nati, Cifukwa canji mwadza naco ca munthu uyu?

30. Anayankha nati kwa iye, Akadakhala wosacita zoipa uyu sitikadampereka iye kwa inu.

31. Ndipo Pilato anati kwa iwo, Mumtenge iye inu, ndi kumweruza iye monga mwa cilamulo canu. Ayuda anati kwa iye, Tiribe ulamuliro wakupha munthu ali yense;

32. kuti mau a Yesu akwaniridwe, amene ananena akuzindikiritsa imfa imene, akuti adzafa nayo.

33. Cifukwa cace Pilato analowanso m'Pretorio, naitana Yesu, nati kwa iye, Iwe ndiwe Mfumu ya Ayuda kodi?

34. Yesu anayankha, Kodi munena ici mwa inu nokha, kapena ena anakuuzani za Ine?

35. Pilato anayankha, ndiri ine Myuda kodi? Mtundu wako ndi ansembe akulu anakupereka kwa ine; wacita ciani?

36. Yesu anayankha, Ufumu wanga suli wa dziko lino lapansi; ufumu wanga ukadakhala wa dziko lino lapansi, anyamata anga akadalimbika nkhondo, kuti ndisaperekedwe kwa Ayuda; koma tsopano ufumu wanga suli wocokera konkuno.

37. Pamenepo Pilato anati kwa iye, Nanga kodi ndiwe Mfumu? Yesu anayankha, Munena kuti ndine Mfumu. Ndinabadwira ici Ine, ndipo ndinadzera ici kudza ku dziko lapansi, kuti ndikacite umboni ndi coonadi. Yense wakukhala mwa coonadi amva mau anga.

38. Pilato ananena kwa iye, Coonadi nciani? Ndipo pamene adanena ici, anaturukiranso kwa Ayudawo, nanena nao, vine sindipeza konse cifukwa mwa iye.

39. Koma muli nao makhalidwe, akuti ndimamasulira inu mmodzi pa Paskha; kodi mufuna tsono kuti ndimasulire inu Mfumu ya Ayuda?

Werengani mutu wathunthu Yohane 18