Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 9:39-50 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

39. Koma Yesu anati, Musamamletsa iye; pakuti palibe munthu adzacita camphamvu m'dzina langa, nadzakhoza msanga kundinenera Ine zoipa.

40. Pakuti iye wosatsutsana ndi ife athandizana nafe.

41. Pakuti munthu ali yense adzakumwetsani inu cikho ca madzi m'dzina langa cifukwa muli ace a Kristu, indetu ndinena ndi inu, kuti iye sadzataya konse mphotho yace.

42. Ndipo yense amene adzalakwitsa kamodzi ka tiana timeneto takukhulupirira Ine, kuli kwabwino kwa iye makamaka kuti mwala waukuru wamphero ukolowekedwe m'khosi mwace, naponyedwe iye m'nyanja.

43. Ndipo ngati dzanja lako likulakwitsa iwe, ulidule: nkwabwino kwa iwe kulowa m'moyo wopunduka dzanja, koposa kukhala ndi manja ako awiri ndi kulowa m'gehena, m'moto wosazima.[

44. ]

45. Ndipo ngati phazi lako likulakwitsa, ulidule; kulowa iwe m'moyo wopunduka mwendo, kuli kwabwino koposa ndi kukhala ndi mapazi ako awiri ndi kuponyedwa m'gehena.[

46. ]

47. Ndipo ngati diso lako likulakwitsa ulikolowole; kulowa iwe m'Ufumu wa Mulungu ndi diso limodzi kuli kwabwino koposa ndi kukhala ndi maso awiri ndi kuponyedwa m'gehena;

48. kumeneko mphutsi yao siikufa, ndi mota suzimidwa.

49. Pakuti onse adzathiridwa mcere wamoto,

50. Mcere uli wabwino; koma ngati mcere unasukuluka, mudzaukoleretsa ndi ciani? Khalani nao mcere mwa inu nokha, ndipo khalani ndi mtendere wina ndi mnzace.

Werengani mutu wathunthu Marko 9