Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 6:8-20 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

8. ndipo anawauza kuti asatenge kanthu ka paulendo, koma ndodo yokha; asatenge mkate, kapena thumba, kapena ndalama m'lamba lao;

9. koma abvale nsapato; ndipo anati, Musabvale malaya awiri.

10. Ndipo ananena nao, Kumene kuli konse mukalowa m'nyumba, khalani komweko kufikira mukacokako.

11. Ndipo pamalo ponse sakulandirani, kapena kumvera inu, pakucoka kumeneko, sansani pfumbi liri ku mapazi anu, likhale mboni ya kwa iwo.

12. Ndipo anaturuka nalalikira kuti anthu atembenuke mitima.

13. Ndipo anaturutsa mizimu yoipa yambiri, nadzoza mafuta anthu ambiri akudwala, nawaciritsa.

14. Ndipo mfumu Herode anamva izi; pakuti dzina lace lidamveka; ndipo ananena, kuti, Yohane Mbatizi wauka kwa akufa, ndipo cifukwa cace mphamvu izi zicitacita mwa Iye.

15. Koma ena ananena, kuti, Ndiye Eliya, Anati enanso, Ndiye mneneri, monga ngati mmodzi wa aneneriwo,

16. Koma Herode pamene anamva, ananena, Yohane amene ndamdula mutu, wauka iyeyo.

17. Pakuti Herode, mwini yekha, adatuma anthu namgwira Yohane, nammanga m'nyumba yandende, cifukwa ca Herodiya, mkazi wa Filipo mbale wace; cifukwa adamkwatira iye.

18. Pakuti Yohane adanena kwa Herode, Si kuloledwa kwa inu kukhala naye mkazi wa mbale wanu.

19. Ndipo Herodiya anamuda, nafuna kumupha; koma sanakhoza;

20. pakuti Herode anaopa Yohane, podziwa kuti ali munthu wolungama ndi woyera mtima, ndipo anamsunga iye. Ndipo pamene anamva iye anathedwa nzeru, oakondwa kumva iye.

Werengani mutu wathunthu Marko 6