Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 12:6-14 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Anamtsalira mmodzi, ndiye mwana wace wokondedwa; potsiriza anamtuma iye kwa iwo, nanena, Adzamcitira ulemu mwana wanga.

7. Koma olima ajawo, ananena mwa iwo okha, Ameneyu ndiye wolowa nyumba; tiyeni timuphe iye, ndipo mundawu udzakhala wathu.

8. Ndipo anamtenga, namupha iye, namtaya kunja kwa munda.

9. Pamenepo mwini munda adzacita ciani? Adzafika, nadzaononga olimawo, nadzapereka mundawo kwa ena.

10. Kodi simunawerenga ngakhale lembo ili;Mwala umene anaukana omanga nyumba,Womwewu unayesedwa mutu wa pangondya:

11. Ici cinacokera kwa Ambuye, Ndipo ciri cozizwitsa m'maso mwathu?

12. Ndipo anayesa kumgwira Iye; koma anaopa khamu la anthu, pakuti anazindikira kuti Iye anakamba fanizo ili kuwatsutsa iwo; ndipo anamsiya Iye, nacoka.

13. Ndipo anatuma kwa Iye ena a Afarisi ndi a Aherode, kuti akamkole Iye m'kulankhula kwace.

14. Ndipo pamene anafika, ananena naye, Mphunzitsi, tidziwa kuti muli woona, ndipo simusamala munthu; pakuti simuyang'ana nkhope ya anthu, koma muphunzitsa njira ya Mulungu moona: Nkuloleka kodi kupereka msonkho kwa Kaisara, kapena iai?

Werengani mutu wathunthu Marko 12