Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Marko 12:1-5 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Ndipo Iye anayamba kulankhula nao m'mafanizo. Munthu analima munda wamphesa, nauzunguniza ndi linga, nakumba moponderamo mphesa, namanga nsanja, naukongoletsa kwa olima munda, namuka kwina.

2. Ndipo m'nyengo yace anatuma kapolo kwa olimawo, kuti alandireko kwa olimawo zipatso za m'munda wamphesa.

3. Ndipo iwo anamtenga iye, nampanda, namcotsa wopanda kanthu.

4. Ndipo anatumanso kapolo wina kwa iwo; ndipo ameneyu anamlasa mutu, namcitira zomcititsa manyazi.

5. Ndipo anatuma wina; iyeyu anamupha; ndi ena ambiri; ena anawapanda, ndi ena anawapha.

Werengani mutu wathunthu Marko 12