Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 6:1-6 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

1. Koma masiku awo, pakucurukitsa ophunzira, kunauka cidandaulo, Aheleniste kudandaula pa Ahebri, popeza amasiye ao anaiwalika pa citumikiro ca tsiku ndi tsiku.

2. Ndipo khumi ndi awiriwo anaitana unyinji wa ophunzira, nati, Sikuyenera kuti ife tisiye mau a Mulungu ndi kutumikira podyerapo.

3. Cifukwa cace, abale, yang'anani mwa inu amuna asanu ndi awiri a mbiri yahwino, odzala ndi Mzimu ndi nzeru, amene tikawaike asunge nchito iyi.

4. Koma ife tidzalimbika m'kupemphera, ndi kutumikira mau.

5. Ndipo mau amene anakonda unyinji wonse; ndipo anasankha Stefano, ndiye munthu wodzala ndi cikhulupiriro ndi Mzimu Woyera, ndi Filipo, ndi Prokoro, ndi Nikanora ndi Timo, ndi Parmena, ndi Nikolao, ndiye wopinduka wa ku Antiokeya:

6. amenewo anawaika pamasopa atumwi; ndipo m'mene adapemphera, anaika manja pa iwo.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 6