Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 4:27-34 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

27. Pakuti zoonadi anasonkhanidwa m'mudzi muno Herode, ndi Pontiyo Pilato yemwe pamodzi ndi amitundu ndi anthu a Israyeli kumcitira coipa Mwana wanu wopatulika Yesu amene munamdzoza;

28. kuti acite ziri zonse dzanja lanu ndi uphungu wanu zidaweruziratu zicitike.

29. Ndipo tsopano Ambuye, penyani mau ao akuopsa, ndipo patsani kwa akapolo anu alankhule mau anu ndi kulimbika mtima konse,

30. m'mene mutambasula dzanja lanu kukaciritsa; ndi kuti zizindikilo ndi zozizwa zicitidwe mwa dzina la Mwana wanu wopatulika Yesu.

31. Ndipo m'mene adapemphera iwo, panagwedezeka pamalo pamene adasonkhanirapo; ndipo anadzazidwa onse ndi Mzimu Woyera, nalankhula mau a Mulungu molimbika mtima.

32. Ndipo unyinji wa iwo akukhulupira anali wa mtima umodzi ndi moyo umodzi; ndipo sananena mmodzi kuti kanthu ka cuma anali naco ndi kace ka iye yekha; koma anali nazo zonse zodyerana.

33. Ndipo atumwi anacita umboni ndi mphamvu yaikulu za kuuka kwa Ambuye Yesu; ndipo panali cisomo cacikuru pa iwo onse.

34. Pakuti mwa iwo munalibe wosowa; 1 pakuti onse amene anali nayo minda, kapena nyumba, anazigulitsa nabwera nao malonda ace a izo adazigulitsa,

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 4