Chipangano Chakale

Chipangano Chatsopano

Macitidwe 26:6-18 Buku Lopatulika 1992 (BL92)

6. Ndipo tsopano ndiimirira pano ndiweruzidwe pa ciyembekezo ca lonjezano limene Mulungu analicita kwa makolo athu;

7. kunkira komweko mafuko athu khumi ndi awiri, potumikira Mulungu kosapumula usiku ndi usana, ayembekeza kufikirako. Cifukwa ca ciyembekezo ici, Mfumu, andinenera Ayuda.

8. Muciyesa cinthu cosakhulupirika, cakuti Mulungu aukitsa akufa?

9. Inedi ndinayesa ndekha, kuti kundiyenera kucita zinthu zambiri zotsutsana nalo dzina la Yesu Mnazarayo.

10. Cimenenso ndinacita m'Yerusalemu: ndipo ndinatsekera ine oyera mtima ambiri m'ndende, popeza ndidalandira ulamuliro wa kwa ansembe akulu; ndiponso pophedwa iwo, ndinabvomerezapo.

11. Ndipo ndinawalanga kawiri kawiri m'masunagoge onse, ndi kuwakakamiza anene zamwano; ndipo pakupsa mtima kwakukuru pa iwo ndinawalondalonda ndi kuwatsata ngakhale kufikira ku midzi yakunja.

12. M'menemo popita ine ku Damasiko ndi ulamuliro ndi ukumu wa kwa ansembe akulu, dzuwa lamsana,

13. ndinaona panjira, Mfumu, kuunika kocokera kumwamba kowalitsa koposa dzuwa, kunawala pondizinga ine ndi iwo akundiperekeza.

14. Ndipo pamene tidagwa pansi tonse, ndinamva mau akunena kwa ine m'cinenedwe ca Cihebri, Saulo, Saulo, undilondalonderanji Ine? nkukubvuta kutsalima pacothwikira.

15. Ndipo ndinati, Ndinu yani Mbuye? Ndipo Ambuye anati, Ine ndine Yesu amene iwe umlondalonda.

16. Komatu uka, imirira pa mapazi ako; pakuti cifukwa ca ici ndinaonekera kwa iwe, kukuika iwe ukhale mtumiki ndi mboni ya izi wandionamo Ine, ndiponso ya izi ndidzakuonekeramo we;

17. ndi kukulanditsa kwa anthu, ndi kwa amitundu, amene Ine ndikutuma kwa iwo,

18. kukawatsegulira maso ao, kuti atembenuke kucokera kumdima, kulinga kukuunika, ndi kucokera ulamuliro wa Satana kulinga kwa Mulungu, kuti alandire iwo cikhululukiro ca macimo, ndi colowa mwa iwo akuyeretsedwa ndi cikhulupiriro ca mwa Ine.

Werengani mutu wathunthu Macitidwe 26